Bakili Muluzi

From Wikipedia

Elesoni Bakili Muluzi, amene anabadwa pa 17 Malichi 1943, anali mtsogoleri wa dziko la Malawi kuyambira 1994 mpaka 2004.

Moyo wawo wakale[Sinthani | sintha gwero]

Muluzi anabadwira mmboma la Mangochi ndipo anagwirako ntchito mmboma. A Muluzi anakhala mmaudindo wosiyana siyana mu chipani cha Malawi Congress Party chomwe chinkalamulira dzikoli.

Utsogoleri wa dziko la Malawi[Sinthani | sintha gwero]

Lernt schreiben, amene ankayimira chipani cha United Democratic Front (UDF) anakhala mtsogoleri wa dzikoli pamene anapambana pa chisankho cha utsogoleri cha zipani zambiri pomwe iwo anapambana ndi 47%. Iwowa anapeza ma voti ambiri kuposa mtsogoleri wa kale amene analamulira dzikoli kuyambira 1964, a Hastings Kamuzu Banda. A Muluzi anapambanso pa chisankho chomwe chinachitika mu 1999 popeza 52% ya mavoti onse, kuwaposa a Gwanda Chakuamba amene ankawoneka ngati apambana pa chisankhocho. Mu 2002, anthu owathandizira ankafuna kusintha malamulo akuti mtsogoleri aziyima pa chisankho kawiri kokha ndi cholinga chakuti a Muluzi ayime kachitatu. Maganizo amenewa anasiyidwa pamene anthu ena anatsutsana nalo ganizoli pochita ziwonetsero. Iwo anasiya boma mu mwezi wa Meyi 2004, ndipo amene anapambana chisankho anali a Bingu wa Muntharika amene ankayimiranso chipani cha UDF.


A Muluzi anali ndi maudindo muboma la a Hastings Kamuzu Banda koma iwo anali mmodzi mwa amene ankatsutsana ndi boma la chipani chimodzi. Ngakhale zinali chonchi, utsogoleri wa a Banda unali ndi nkhani zina zosakhala bwino, mwachitsanzo pamene iwo anagulitsa chimanga chomwe dzikoli linkasunga pa nthawi yomwe kunali njala komanso posokoneza ndalama zomwe zinapezeka pa malonda ndi maiko ena a chimangacho, ngakhale maiko ena akunja ankayesayesa kuti afufuze chomwe chinachitika. Anthu ambiri amaganiza kuti ndalamazi anagawana a Muluzi ndi wotsatira awo ndipo zinasungidwa ku nyumba zosungirako ndalama za maiko a kunja. Ngakhale kunali nkhani zambiri zotele, a Muluzi anali mtsogoleri wotchuka mu dzikolu makamaka ku madera a ku mmwela kwa dzikoli.

links[Sinthani | sintha gwero]

Moyo wawo atasiya utsogoleri[Sinthani | sintha gwero]

Iwo anapitiliza kukhala mtsogoleri wa UDF ngakhale anasemphana maganizo ndi amene iwo anamusankha kukhala mtsogoleri, a Bingu wa Muntharika. A Muntharika anasiya chipani cha UDF ndikukapanga chipani chawo cha Democractic Progressive Party (DPP).


A Muluzi anamangidwa pa 27 Julaye 2006 pa milandu yokhudza ziphuphu koma anamasulidwa tsiku lomwelo. Patangopita ma ola ochepa, munthu amene ankafufuza za mulandu wa a Muluzi, a Gustav Kaliwo anaimitsidwa pa ntchito ndi a Muntharika. Pa chifukwa chimenechi, amene amazenga mulandu wa a Muluzi, a Ishmael Wadi anaimitsa mulanduwu.


Kuyambira mwezi wa Malichi 2007 anthu ena anayamba kunena kuti a Muluzi adzaimenso pa chisankho chomwe chidzachitike mu 2009 ndipo anawapatsa nthawi yakuti anene ngati ankafuna kudzaima pa chisankhocho. Pa 11 Malichi, a Muluzi analengeza kuti adzaimadi, ndipo otsatira awo ena ngati a Brown Mpinganjira komanso a Sam Mpasu, amene koyambilira ankafuna kudzaimira UDF pa chisankhochi, analengeza kuti sadzaima chifukwa cha chidwi chomwe a Muluzi anawonetsa kudzaima.


Ngakhale zili chonchi, pali kusamvetsetsa pa zomwe malamulo a dzikoli amanena zokhudza kuima pa chisankho cha atsogoleri akale chifukwa malamulowo amanena kuto mtsogoleri sangaime kachitatu kotsatizana ndipo a Muluzi akufuna kuima chifukwa sanaime pa chisankho chomwe chinachitika 2004. Pa chifukwa chimenechi, anthu ambiri akufuna kuti malamulowo asinthidwe ndipo kuti mawu onena zotsatizana achotsedwe mu malamulowo.