Jump to content

Jean Claude Van Damme

Kuchokera ku Wikipedia

Van Damme ndiopanga mafilimu waku America. Iyeyu anabadwa Jean-Claude Camille Van Varenberg ku Berchem-Sainte-Agathe, Brussels, Belgium, kwa Eliana ndi Eugène Van Varenberg, wowerengera ndalama. "Minofu ya ku Brussels" inayamba masewera a karati ali ndi zaka khumi ndi chimodzi. Bambo ake adamuwonetsa ku masewera a karati pamene adawona mwana wake ali wofooka mwakuthupi. Ali ndi zaka 12, Van Damme anayamba maphunziro ake a karati ku Center National De Karate (National Center of Karate) motsogoleredwa ndi Master Claude Goetz ku Ixelles, Belgium. Van Damme adaphunzitsidwa kwa zaka 4 ndipo adapeza malo ku Belgium Karate Team. Anapambana mpikisano wa karate wa European professional karate ali wachinyamata, ndipo adagonjetsanso womenyera karate wachiwiri padziko lonse lapansi. Cholinga chake chinali kukhala nambala wani koma adasokonekera pamene adachoka kumudzi kwawo ku Brussels. Mu 1976 ali ndi zaka khumi ndi zisanu ndi chimodzi, Jean-Claude adayamba ntchito yake yankhondo.